1 Kings 1:38 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso Akereti ndi Apeleti oteteza mfumu aja, adapita nakamkweza Solomoni pa bulu wa mfumu Davide, kupita naye ku Gihoni.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo Zadoki wansembe, ndi Natani mneneri, ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndi Akereti, ndi Apeleti aja anatsika, nakweza Solomoni pa nyuru ya mfumu Davide, nafika naye ku Gihoni.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo Zadoki wansembe, ndi Natani mneneri, ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndi Akereti, ndi Apeleti aja anatsika, nakweza Solomo pa nyuru ya mfumu Davide, nafika naye ku Gihoni.