1 Kings 1:53 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kenaka mfumu Solomoni adatuma anthu kukamtenga Adoniya kuguwa kuja. Iye adabwera kudzalambira mfumu Solomoni. Ndipo Solomoni adamuuza kuti, “Chabwino, ungathe kupita kunyumba kwako.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Tsono mfumu Solomoni anatuma anthu nakamtsitsa ku guwa la nsembe. Iye nadza, nagwadira mfumu Solomoni; Solomoni nati kwa iye, Pita kwanu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Tsono mfumu Solomo anatuma anthu nakamtsitsa ku guwa la nsembe. Iye nadza, nagwadira mfumu Solomo; Solomo nati kwa iye, Pita kwanu.