1 Kings 17:13 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma Eliya adauza maiyo kuti, “Musade nkhaŵa. Pitani, mukachite monga mwaneneramo. Koma poyamba mutapeko kaufa pang'ono, mundiphikire kakeke, mubwere nako kuno. Pambuyo pake mukaphikenso kuti mudye inuyo ndi mwana wanu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Eliya anati kwa iye, Usachita mantha, kachite monga umo wanenamo, koma thanga wandiocherako kamkate, nubwere nako kwa ine; ndipo utatero udziphikire wekha ndi mwana wako.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Eliya anati kwa iye, “Musachite mantha. Pitani mukachite monga mwaneneramo. Koma poyamba mundipangire kachakudya pangʼono kuchokera pa ufa umene muli nawo ndi kubwera nako kwa ine, ndipo kenaka mukaphike choti mudye inuyo ndi mwana wanuyo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Eliya anati kwa iye, Usacita mantha, kacite monga umo wanenamo, koma thanga wandiocerako kamkate, nubwere nako kwa ine; ndipo utatero udziphikire wekha ndi mwana wako.