1 Kings 18:26 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Iwowo adatenga ng'ombe yamphongo imene adaŵapatsa, naipha. Tsono adatama dzina la Baala mopemba, kuyambira m'maŵa mpaka masana, ponena kuti, “Inu a Baala, tiyankheni ife.” Aneneri a Baala aja ankalumphalumpha movina, kuzungulira guwa limene adaamangalo, koma sipadamveke ndi liwu lomwe, panalibe woyankha.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo iwo anatenga ng'ombe ija adawapatsa, naikonza, naitana dzina la Baala, kuyambira m'mawa kufikira pausana, nati, Baala, timvereni ife. Koma panalibe mau kapena wovomereza. Ndipo anavinavina kuguwa adalimanga.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Choncho iwo anatenga ngʼombe yayimunayo imene anawapatsa, nayikonza. Kenaka anayitana dzina la Baala kuyambira mmawa mpaka masana. Iwo anafuwula kuti, “Inu Baala, tiyankheni ife.” Koma panalibe yankho; palibe amene anayankha. Ndipo anavinavina mozungulira guwa lansembe limene anapanga.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo iwo anatenga ng'ombe ija adawapatsa, naikonza, naitana dzina la Baala, kuyambira m'mawa kufikira pausana, nati, Baala, timvereni ife. Koma panalibe mau kapena wobvomereza. Ndipo anabvinabvina kuguwa adalimanga.