1 Kings 18:33 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Adaika nkhuni zija m'malo mwake, nadula ng'ombe ija nthulinthuli, nkuika nthulizo pankhunipo. Pambuyo pake adauza anthu kuti, “Dzazani mitsuko inai ndi madzi, muŵathire pa nyama yansembeyo, ndi pa nkhunizo.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo anakonza nkhunizo, naduladula ng'ombe, naiika pankhuni. Nati, Dzazani madzi mbiya zinai, muwathire pa nsembe yopsereza ndi pankhuni.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Anayika nkhuni zija mʼmalo mwake nadula nthulinthuli ngʼombe yayimuna ija ndi kuyika nthulizo pa nkhunipo. Pamenepo Eliya anati, “Dzazani mitsuko inayi ndi madzi ndipo muwathire pa nyama ya nsembeyo ndi nkhunizo.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo anakonza nkhunizo, naduladula ng'ombe, naiika pankhuni. Nati, Dzazani madzi mbiya zinai, muwathire pa nsembe yopsereza ndi pankhuni.