1 Kings 18:7 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamene Obadiya ankapita pa ulendo wake, adangoona mneneri Eliya akubwera kudzakumana naye. Obadiya adamzindikira Eliyayo, ndipo adamuŵeramira, namufunsa kuti, “Kodi ndinudi mbuyanga Eliya?”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Obadiya ali m'njira taona, Eliya anakomana naye; iye namdziwa, namgwadira, nati, Ndinu kodi mbuye wanga Eliya?
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Obadiya akuyenda mʼnjira anakumana ndi Eliya. Ndipo taonani, Obadiya anamuzindikira Eliyayo, naweramira pansi ndipo anati, “Kodi ndinu, mbuye wanga Eliya?”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Obadiya ali m'njira, taona, Eliya anakomana naye; iye namdziwa, namgwadira, nati, Ndinu kodi mbuye wanga Eliya?