1 Kings 2:26 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono mfumu idauza wansembe Abiyatara kuti, “Pita ku Anatoti ku minda yako. Uyenera kufa ndithu, koma sindikupha tsopano lino ai, chifukwa udasunga Bokosi lachipangano la Chauta pamaso pa Davide bambo wanga, ndiponso poti udazunzika naye limodzi bambo wanga.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo mfumu inanena ndi Abiyatara wansembeyo, Pita ku Anatoti ku minda yako; pakuti wakutidwa ndi imfa; koma sindikupha iwe lero lino, chifukwa unanyamula likasa la Ambuye Yehova pamaso pa Davide atate wanga, ndi popeza unanzunzidwa monse umo atate wanga Davide anazunzidwamo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo mfumu inanena ndi Abyatara wansembeyo, Pita ku Anatoti ku minda yako; pakuti wakutidwa ndi imfa; koma sindikupha iwe lero lino, cifukwa unanyamula likasa la Ambuye Yehova pamaso pa Davide atate wanga, ndi popeza unazunzidwa monse umo atate wanga Davide anazunzidwamo.