1 Samuel 1:11 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Adalumbira kuti, “Inu Chauta Wamphamvuzonse, muyang'ane kuzunzika kwanga ndipo muyankhe pemphero langa, osandiiŵala ine mdzakazi wanu. Ndithu mukandipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzampereka mwanayo kwa Inu Chauta masiku onse a moyo wake, ndipo pamutu pake sipadzapita lumo.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
nalonjeza chowinda, nati, Yehova wa makamu, mukapenyera ndithu kusauka kwa mdzakazi wanu, ndi kukumbukira ine, ndi kusaiwala mdzakazi wanu, mukapatsa mdzakazi wanu mwana wamwamuna, ine ndidzampereka kwa Yehova masiku onse a moyo wake, ndipo palibe lumo lidzapita pamutu pake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
nalonjeza cowinda, nati, Yehova wa makamu, mukapenyera ndithu kusauka kwa mdzakazi wanu, ndi kukumbukila ine, ndi kusaiwala mdzakazi wanu, mukapatsa mdzakazi wanu mwana wamwamuna, ine ndidzampereka kwa Yehova masiku onse a moyo wace, ndipo palibe lumo lidzapita pamutu pace.