1 Samuel 10:24 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono Samuele adafunsa anthu onsewo kuti, “Kodi mukumuwona munthu amene Chauta wamsankha? Palibe wina wonga ameneyu pakati pa anthu onse.” Ndipo anthu onse adafuula kuti, “Amfumu akhale ndi moyo wautali!”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Samuele ananena ndi anthu onse, Mumuona kodi iye amene Yehova anamsankha, kuti palibe wina wakufanana naye pakati pa anthu onse? Ndipo anthu onse anafuula, kuti, Akhale ndi moyo mfumuyo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Samueli anafunsa anthu onse kuti, “Kodi mukumuona munthu amene Yehova wasankha? Palibe wofanana naye pakati pa anthu onse.” Kenaka anthu onse anafuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Samueli ananena ndi anthu onse, Mumuona kodi iye amene Yehova anamsankha, kuti palibe wina wakufanana naye pakati pa anthu onse? Ndipo anthu onse anapfuula, kuti, Akhale ndi moyo mfumuyo.