1 Samuel 13:14 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Chauta wadzifunira yekha munthu wa kumtima kwake. Chauta wamsankha munthuyo kuti akhale mfumu yolamulira anthu ake, chifukwa inu simudatsate zimene Iye adakulamulani.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma tsopano ufumu wanu sudzakhala chikhalire; Yehova wadzifunira munthu wa pamtima pake; ndipo Yehova wamuika iye akhale mtsogoleri wa anthu ake, chifukwa inu simunasunga chimene Yehova anakulamulirani.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Yehova wapeza munthu wapamtima pake ndipo wamusankha kukhala mtsogoleri wa anthu ake chifukwa inu simunasunge malamulo a Yehova.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma tsopano ufumu wanu sudzakhala cikhalire; Yehova wadzifunira munthu wa pamtima pace; ndipo Yehova wamuika iye akhale mtsogoleri wa anthu ace, cifukwa inu simunasunga cimene Yehova anakulamulirani.