1 Samuel 14:21 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Ahebri ena amene kale adaali pamodzi ndi Afilistiwo, ndipo anali atapita nao ku zithandozo, iwonso adatembenuka nakhala pamodzi ndi Aisraele a mbali ya Saulo ndi Yonatani.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndiponso Ahebri akukhala nao Afilisti kale, amene anatuluka m'dziko lozungulira kukalowa nao kuzithando; iwonso anatembenukira kuti akakhale ndi Aisraele amene anali ndi Saulo ndi Yonatani.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Aheberi ena amene kale anali ndi Afilisti mpaka kukakhala ku misasa yawo, iwonso anatembenuka nakhala pamodzi ndi Aisraeli amene ankatsata Sauli ndi Yonatani.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndiponso Ahebri akukhala nao Afilisti kale, amene anaturuka m'dziko lozungulira kukaiowa nao kuzithando; iwonso anatembenukira kuti akakhale ndi Aisrayeli amene anali ndi Sauli ndi Jonatani.