1 Samuel 14:33 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma ena adauza Saulo kuti, “Onani, anthu akuchimwira Chauta podyera kumodzi ndi magazi.” Saulo adati, “Mwaukira Chauta lero! Pezani mwala waukulu muukunkhunizire kuno.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo anauza Saulo, kuti, Onani anthu alikuchimwira Yehova, umo akudya zamwazi. Ndipo iye anati, Munachita konyenga; kunkhunizani mwala waukulu kwa ine lero.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma anthu ena anawuza Sauli kuti, “Taona anthu akuchimwira Yehova pakudya nyama yomwe ili ndi magazi.” Ndipo Sauli anati, “Mwaonetsa kusakhulupirika. Tsopano gubuduzirani mwala waukulu pano.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo anauza Sauli, kuti, Onani anthu alikucimwira Yehova, umo akudya zamwazi. Ndipo iye anati, Munacita konyenga; kunkhunizani mwala waukuru kwa ine lero.