1 Samuel 15:1 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsiku lina Samuele adauza Saulo kuti, “Paja Chauta adaatuma ine kuti ndikudzozeni, kuti mukhale mfumu ya anthu ake Aisraele. Nchifukwa chake tsono imvani uthenga wochokera kwa Chauta.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Samuele ananena ndi Saulo, Yehova ananditumiza ine kukudzozani mukhale mfumu ya anthu ake Aisraele; chifukwa chake tsono mumvere kunena kwa mau a Yehova.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Samueli anawuza Sauli kuti, “Yehova anandituma ine kuti ndikudzozeni kukhala mfumu ya anthu ake, Aisraeli. Tsopano imvani zimene Yehova akunena.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Samueli ananena ndi Sauli, Yehova ananditumiza ine kukudzozani mukhale mfumu ya anthu ace Aisrayeli; cifukwa cace tsono mumvere kunena kwa mau a Yehova.