1 Samuel 22:14 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma Ahimeleki adayankha mofunsa kuti, “Amfumu, kodi ndani pakati pa ankhondo anu amene ali wokhulupirika ngati Davide? Iye uja ndi mkamwini wanu, mtsogoleri wa gulu lanu lokutchinjirizani, ndiponso munthu wolemekezeka m'banja mwanu?
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Ahimeleki anayankha mfumu, nati, Ndipo ndani mwa anyamata anu onse ali wokhulupirika ngati Davide amene, mkamwini wa mfumu; wakuyenda mu uphungu wanu, nalemekezeka m'nyumba mwanu?
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ahimeleki anayankha mfumu kuti, “Kodi ndani mwa ankhondo anu onse amene ali wokhulupirika monga Davide? Iye uja ndi mkamwini wa mfumu, kapitawo wa asilikali okutetezani ndiponso munthu amene amalemekezedwa mʼbanja lanu?
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Ahimeleki anayankha mfumu, nati, Ndipo ndani mwa anyamata anu onse ali wokhulupirika ngati Davide amene, mkamwini wa mfumu; wakuyenda mu uphungu wanu, nalemekezeka m'nyumba mwanu?