1 Samuel 26:21 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono Saulo adati, “Ndachimwa. Bwerera, mwana wanga Davide, sindidzakuchitanso choipa, popeza kuti moyo wanga wauwona ngati wa mtengo wapatali. Ndithu ndachita zauchitsiru ndipo ndachimwa kwambiri.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo Saulo anati, Ndinachimwa; bwera, mwana wanga Davide; pakuti sindidzakuchitiranso choipa, popeza moyo wanga unali wa mtengo wapatali pamaso pako lero; ona, ndinapusa ndi kulakwa kwakukulu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndipo Sauli anati, “Ine ndachimwa. Bwerera mwana wanga Davide. Sindidzakuchitanso choyipa popeza lero wauwona moyo wanga ngati wamtengowapatali. Taona, ndachita zauchitsiru ndipo ndachimwa kwambiri.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo Sauli anati, Ndinacimwa; bwera, mwana wanga Davide; pakuti sindidzakucitiranso coipa, popeza moyo wanga unati wa mtengo wapatali pamaso pako lero; ona, ndinapusa ndi kulakwa kwakukuru.