1 Samuel 26:25 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Apo Saulo adauza Davide kuti, “Mulungu akudalitse mwana wanga Davide. Udzachita zazikulu, ndipo pa zonsezo udzapambana.” Choncho Davide adachokapo, ndipo Saulo adabwerera kwao.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pomwepo Saulo anati kwa Davide, Udalitsike iwe, mwana wanga Davide; udzachita ndithu champhamvu, nudzapambana. Chomwecho Davide anamuka, ndipo Saulo anabwera kwao.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndipo Sauli anawuza Davide kuti, “Yehova akudalitse iwe Davide mwana wanga. Udzachita zinthu zazikulu ndipo udzapambana.” Choncho Davide anayenda njira yake ndipo Sauli anabwerera kwawo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pomwepo Sauli anati kwa Davide, Udalitsike iwe, mwana wanga Davide; udzacita ndithu camphamvu, nudzapambana. Comweco Davide anamuka, ndipo Sauli anabwera kwao.