1 Samuel 26:7 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Choncho Davide ndi Abisai adakaloŵa ku zithando zankhondo usiku. Saulo anali gone m'chithando chake, atazika mkondo wake pansi cha kumutu kwake. Abinere ndi ankhondo onse adaagona momzungulira.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Chomwecho Davide ndi Abisai anafika kwa anthuwo usiku; ndipo onani, Saulo anagona tulo m'kati mwa linga la magaleta, ndi mkondo wake wozika kumutu kwake; ndi Abinere ndi anthuwo anagona pomzinga iye.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Choncho Davide ndi Abisai anapita ku misasa ya ankhondowo usiku. Atafika anangopeza Sauli ali gone mu msasa wake mkondo wake atawuzika pansi pafupi ndi mutu wake, Abineri ndi ankhondo onse anali atagona momuzungulira.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Comweco Davide ndi Abisai anafika kwa anthuwo usiku; ndipo onani, Sauli anagona tulo m'kati mwa linga la magareta, ndi mkondo wace wozika kumutu kwace; ndi Abineri ndi anthuwo anagona pomzinga iye.