1 Samuel 29:3 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamenepo atsogoleri aja a Afilisti adafunsa kuti, “Kodi Ahebriŵa akuchita chiyani kuno?” Akisi adayankha kuti, “Uyutu ndi Davide, mtumiki wa Saulo mfumu ya Aisraele. Iye wakhala nane tsopano masiku ambiri kapena nditi zaka, chibwerere chake kuno sindidampeze cholakwa chilichonse mpaka lero lino.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo akalonga a Afilisti anati, Ahebri awa achitanji pano? Ndipo Akisi ananena kwa akalonga a Afilisti, Uyu si Davide uja mnyamata wa Saulo, mfumu ya Israele, amene wakhala nane masiku awa kapena zaka izi, ndipo sindinapeza kulakwa mwa iye, kuyambira tsiku lija anaphatikana nane kufikira lero.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo akalonga a Afilisti anati, Ahebri awa acitanji pano? Ndipo Akisi ananena kwa akalonga a Afilisti, Uyu si Davide uja mnyamata wa Sauli, mfumu ya Israyeli, amene wakhala nane masiku awa kapena zaka izi, ndipo sindinapeza kulakwa mwa iye, kuyambira tsiku lija anaphatikana nane kufikira lero.