1 Samuel 6:14 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Galeta lija lidafikira ku munda wa Yoswa ku Betesemesi ndi kuima komweko. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu am'mudzimo adaliŵaza nkhuni galetalo ndipo adapha ng'ombezo nazipereka kwa Chauta ngati nsembe yopsereza.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo galetalo linafika m'munda wa Yoswa wa ku Betesemesi, ndi kuima momwemo, pa mwala waukulu; ndipo anawaza matabwa a galetalo, nazipereka ng'ombezo nsembe yopsereza kwa Yehova.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Galeta lija linafika ku munda wa Yoswa ku Beti-Semesi ndipo linayima. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu anawaza nkhuni galetalo, ndipo anapha ngʼombe zija ndi kuzipereka ngati nsembe zopsereza kwa Yehova.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo garetalo linafika m'munda wa Yoswa wa ku Betisemesi, ndi kuima momwemo, pa mwala waukuru; ndipo anawaza matabwa a garetalo, nazipereka ng'ombezo nsembe yopsereza kwa Yehova.