1 Samuel 6:3 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Iwo adati, “Mukafuna kubwezera Bokosili, musalitumize lopanda kanthu, koma mwa njira iliyonse mulitumize pamodzi ndi mphatso, kuti ikhale nsembe yopepesera machimo. Pambuyo pake mudzachira, ndipo pamenepo mudzadziŵa chifukwa chiyani chilango cha Mulungu sichikukuchokani.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo iwo anati, Ngati mulitumiza kwina likasa la Mulungu wa Israele, musalitumize lopanda kanthu; koma makamaka mulibweze ndi nsembe yopalamula, mukatero mudzachiritsidwa, ndi kudziwa chifukwa chake dzanja lake lili pa inu losachoka.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Iwo anayankha kuti, “Ngati mufuna kubweza Bokosi la Mulungu wa Israeli, musalitumize wopanda kanthu, koma muyesetse kulitumiza pamodzi ndi nsembe yopepesera machimo. Mukatero mudzachiritsidwa, ndipo mudzadziwa chifukwa chiyani chilango cha Yehova sichikukuchokani.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo iwo anati, Ngati mulitumiza kwina likasa la Mulungu wa Israyeli, musalitumize lopanda kanthu; koma makamaka mulibweze ndi nsembe yoparamula, mukatero mudzaciritsidwa, ndi kudziwa cifukwa cace dzanja lace liri pa inu losacoka.