1 Timothy 5:21 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamaso pa Mulungu, pamaso pa Khristu Yesu, ndi pamaso pa angelo onse osankhidwa, ndikukulamula ndithu kuti uzitsata malamulo ameneŵa mopanda tsankho, ndipo kuti usachite chilichonse mokondera.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndikuchitira umboni pamaso pa Mulungu, ndi Khristu Yesu, ndi angelo osankhika, kuti usunge izi kopanda kusankhiratu, wosachita kanthu monga mwa tsankho.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndikukulamulira pamaso pa Mulungu, pamaso pa Yesu Khristu ndi pamaso pa angelo osankhika, kuti usunge malangizowa mosachotsera ndipo usachite kalikonse mokondera.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndikucitira umboni pamaso pa Mulungu, ndi Kristu Yesu, ndi angelo osankhika, kuti usunge izi kopanda kusankhiratu, wosacita kanthu monga mwa tsankhu.