2 Chronicles 23:3 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Msonkhano wonsewo udachita chipangano ndi mfumu m'Nyumba ya Mulungu. Yehoyada adaŵauza anthuwo kuti, “Nayu mwana wa mfumu. Iyeyu akhale mfumu monga Chauta adanenera za ana a Davide.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo msonkhano wonse unapangana pangano ndi mfumu m'nyumba ya Mulungu. Ndipo ananena nao, Taonani, mwana wa mfumu adzakhala mfumu monga Yehova ananena za ana a Davide.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo msonkhano wonse unapangana pangano ndi mfumu m'nyumba ya Mulungu. Ndipo ananena nao, Taonani, mwana wa mfumu adzakhala mfumu monga Yehova ananena za ana a Davide.