2 Chronicles 31:11 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono Hezekiya adaŵalamula anthuwo kuti akonze zipinda za ku Nyumba ya Chauta. Iwo adakonzadi zipindazo.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo Hezekiya anawauza akonze zipinda m'nyumba ya Yehova; nazikonza.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo Hezekiya anawauza akonze zipinda m'nyumba ya Yehova; nazikonza.