2 Chronicles 34:33 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kenaka Yosiya adachotsa zinthu zonyansa zonse ku maiko onse a Aisraele, nakakamiza anthu onse okhala ku Israele kuti azitumikira Chauta, Mulungu wao. Motero anthuwo sadaleke kutsata Chauta, Mulungu wa makolo ao, pa masiku onse a Yosiya.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Yosiya nachotsa zonyansa zonse m'maiko onse okhala a ana a Israele, natumikiritsa onse opezeka m'Israele, inde kutumikira Yehova Mulungu wao. Masiku ake onse iwo sanapatuke kusamtsata Yehova Mulungu wa makolo ao.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yosiya anachotsa mafano onse onyansa mʼdziko lonse limene linali la Aisraeli ndipo anawuza onse amene anali mu Israeli kutumikira Yehova Mulungu wawo. Pa masiku onse a moyo wake, iye sanaleke kutsatira Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Yosiya nacotsa zonyansa zonse m'maiko onse okhala a ana a Israyeli, natumikiritsa onse opezeka m'lsrayeli, inde kutumikira Yehova Mulungu wao. Masiku ace onse iwo sanapambuka kusamtsata Yehova Mulungu wa makolo ao.