2 Corinthians 1:19 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu, amene ine ndi Silivano ndi Timoteo tidakulalikirani, sanali “Inde” ndiponso “Ai” pa nthaŵi imodzi, koma nthaŵi zonse anali “Inde” wa Mulungu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pakuti Mwana wa Mulungu, Yesu Khristu, amene analalikidwa mwa inu ndi ife, (ine ndi Silivano ndi Timoteo) sanakhala eya ndi iai, koma anakhala eya mwa Iye.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Pakuti Yesu Khristu mwana wa Mulungu amene ine, Silivano ndi Timoteyo tinamulalikira pakati panu sali “Inde” yemweyonso “Ayi.” Koma nthawi zonse mwa Iye muli “Inde.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pakuti Mwana wa Mulungu, Yesu Kristu, amene analalikidwa mwa inu ndi ife, (ine ndi Silvano ndi Timoteo) sanakhala eya ndi iai, koma anakhala eya mwa iye.