2 Corinthians 11:16 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Ndikufuna kubwerezanso kuti munthu wina aliyense asandiyese wopusa. Koma ngati inuyo mukundiyesadi wopusa, chabwino mundilandire ngati chitsiru, kuti inenso ndinyadirepo.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndinenanso, Munthu asandiyese wopanda nzeru; koma ngati mutero, mundilandirenso ine monga wopanda nzeru, kuti inenso ndidzitamandire pang'ono.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndibwereze kunena kuti, wina aliyense asandiyese chitsiru. Koma ngati mutero, mundilandire monga mmene mukhoza kulandirira chitsiru, kuti ndinyadirepo pangʼono.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndinenanso, Munthu asandiyese wopanda nzeru; koma ngati mutero, mundilandirenso ine monga wopanda nzeru, kuti inenso ndidzitamandire pang'ono.