2 Corinthians 4:7 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma ife ndife mbiya zadothi chabe zosungiramo chumachi, kuti padziŵike kuti mphamvu zazikulu zoterezi ndi za Mulungu, osati zathu ai.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma tili nacho chuma ichi m'zotengera zadothi, kuti ukulu woposa wamphamvu ukhale wa Mulungu, wosachokera kwa ife;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma tili ndi chuma ichi mʼmbiya zadothi, kusonyeza kuti mphamvu yoposayi, imachokera kwa Mulungu osati kwa ife.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma tiri naco cuma ici m'zotengera zadothi, kuti ukulu woposa wamphamvu ukhale wa Mulungu, wosacokera kwa ife;