2 Kings 14:10 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Inde iwe wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza. Badzitamira kupambana kwakoko, koma ai tsono khala kwanu komweko. Bwanji ukufuna kuutsa mavuto dala? Bwinotu ungagwe, iweyo pamodzi ndi anthu a ku Yuda.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Wakanthadi Aedomu, koma mtima wako wakukweza; ulemekezeke, nukhale kwanu; udziutsiranji tsoka, ungagwe iwe ndi Yuda pamodzi nawe;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Wakanthadi Aedomu, koma mtima wako wakukweza; ulemekezeke, nukhale kwanu; udziutsiranji tsoka, ungagwe iwe ndi Yuda pamodzi nawe;