2 Kings 17:13 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Monsemo Chauta adatuma amithenga ndi aneneri ake ku Israele ndi ku Yuda, okalalika kuti, “Musinthe makhalidwe anu auchimo ndipo mumvere Malamulo anga amene ndidaŵapereka kwa makolo anu, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Yehova anachitira umboni Israele ndi Yuda mwa dzanja la mneneri aliyense, ndi mlauli aliyense, ndi kuti, Bwererani kuleka ntchito zanu zoipa, nimusunge malamulo anga ndi malemba anga, monga mwa chilamulo chonse ndinachilamulira makolo anu, ndi kuchitumizira inu mwa dzanja la atumiki anga aneneri.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yehova anachenjeza Israeli ndi Yuda kudzera mwa aneneri ake onse ndi alosi kuti, “Lekani mchitidwe wanu woyipawo. Mverani malamulo anga ndi malangizo anga potsatira zonse zolembedwa mʼmalamulo a Mose, zimene ndinalamulira makolo anu kuti azimvere, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Yehova anacitira umboni Israyeli ndi Yuda mwa dzanja la mneneri ali yense, ndi mlauli ali yense, ndi kuti, Bwererani kuleka nchito zanu zoipa, nimusunge malamulo anga ndi malemba anga, monga mwa cilamulo conse ndinacilamulira makolo anu, ndi kucitumizira inu mwa dzanja la atumiki anga aneneri.