2 Kings 4:1 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsiku lina mkazi wa mmodzi wa m'gulu la aneneri adapita kwa Elisa. Adampempha mokweza kuti, “Mwamuna wanga, amene anali mtumiki wanu, adamwalira. Ndipo inu mukudziŵa kuti mtumiki wanuyo ankaopa Chauta. Tsono kwafika munthu amene mwamuna wanga adakongola zinthu zake, ndipo akuti atenge ana anga aŵiri, kuti akhale akapolo ake chifukwa cha ngongoleyo.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo wina wa akazi a ana a aneneri anafuula kwa Elisa, ndi kuti, Mnyamata wanu, mwamuna wanga wafa; mudziwa kuti mnyamata wanu anaopa Yehova; ndipo wafika wamangawa kunditengera ana anga awiri akhale akapolo ake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Mkazi wa mmodzi mwa ana a aneneri anafuwula kwa Elisa kuti, “Mtumiki wanu, mwamuna wanga wamwalira ndipo inu mukudziwa kuti ankaopa Yehova. Koma tsopano munthu amene mwamuna wanga anakongolako zinthu zake, akubwera kudzatenga ana anga awiri aamuna kuti akhale akapolo ake.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo wina wa akazi a ana a aneneri anapfuula kwa Elisa, ndi kuti, Mnyamata wanu, mwamuna wanga wafa; mudziwa kuti mnyamata wanu anaopa Yehova; ndipo wafika wamangawa kunditengera ana anga awiri akhale akapolo ace.