2 Kings 4:38 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pambuyo pake Elisa adabwereranso ku Giligala, ndipo m'dzikomo munali njala. Tsiku lina Elisa ankaphunzitsa gulu la aneneri, ndipo patapita nthaŵi, adauza mtumiki wake kuti, “Ikapo nkhali yaikulu pa moto, uŵaphikire chakudya a m'gulu la aneneriŵa.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Elisa anabwera ku Giligala, koma m'dzikomo munali njala; ndi ana a aneneri anali kukhala pansi pamaso pake; ndipo anati kwa mnyamata wake, Ika nkhali yaikuluyo, uphikire ana a aneneri.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Elisa anabwerera ku Giligala ndipo ku dera limenelo kunali njala. Elisa akukumana ndi ana a aneneri, anati kwa mtumiki wake, “Ika mʼphika waukulu pa moto ndipo uwaphikire chakudya anthu awa.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Elisa anabwera ku Giligala, koma m'dzikomo munali njala; ndi ana a aneneri anali kukhala pansi pamaso pace; ndipo anati kwa mnyamata wace, Ika nkhali yaikuruyo, uphikire ana a aneneri.