2 Kings 8:12 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono Hazaele adamufunsa kuti, “Mbuyanga, mukuliranji?” Iyeyo adayankha kuti, “Chifukwa ndikudziŵa zoipa zimene mudzaŵachita Aisraele. Mudzatentha malinga ao ankhondo ndipo mudzapha ankhondo ao ambiri. Mudzapondereza tiana tao, ndipo mudzang'amba akazi ao apakati.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Nati Hazaele, Muliriranji, mbuye wanga? Nayankha iye, Popeza ndidziwa choipa udzachitira ana a Israele; udzatentha malinga ao ndi moto, nudzapha anyamata ao ndi lupanga, nudzaphwanya makanda ao, nudzang'amba akazi ao okhala ndi pakati.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?” Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Nati Hazaeli, Muliriranji, mbuye wanga? Nayankha iye, Popeza ndidziwa coipa udzacitira ana a Israyeli; udzatentha malinga ao ndi moto, nudzapha anyamata ao ndi lupanga, nudzaphwanya makanda ao, nudzang'amba akazi ao okhala ndi pakati.