2 Samuel 13:6 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Choncho Aminoni adagona, nachita ngati wadwala. Mfumu itabwera kudzamuwona, Aminoniyo adauza mfumuyo kuti, “Chonde, mulole mlongo wanga Tamara abwere, kuti adzandiphikire chakudya ine ndikupenya, kuti ndidzadyere m'manja mwake.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Chomwecho Aminoni anagona, nadzikokomeza alikudwala; ndipo pamene mfumu inadza kumuona, Aminoni anati kwa mfumuyo, Mulole Tamara mlongo wanga abwere ndi kundipangira timitanda tiwiri pamaso panga, kuti ndikadye cha m'manja mwake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Kotero Amnoni anagona nakhala ngati akudwala. Mfumu itabwera kudzamuona, Amnoni anati kwa iyo, “Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara kuti abwere adzandipangire buledi wapamwamba ineyo ndikuona, kuti ndidye ali mʼmanja mwake.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Comweco Amnoni anagona, nadzikokomeza alikudwala; ndipo pamene mfumu inadza kumuona, Amnoni anati kwa mfumuyo, Mulole Tamara mlongo wanga abwere ndi kundipangira timitanda tiwiri pamaso panga, kuti ndikadye ca m'manja mwace.