2 Samuel 14:2 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono adatuma anthu ku Tekowa kukatengako mkazi wanzeru kumeneko. Adauza mkaziyo kuti, “Ukhale ngati mfedwa, uvale zovala zaumasiye. Usadzole mafuta, koma ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Yowabu anatumiza ku Tekowa, natenga kumeneko mkazi wanzeru, nanena naye, Ukokomezeke monga mfedwa, nuvale zovala za pamaliro, osadzola mafuta, koma ukhale ngati munthu wamkazi wakulira akufa nthawi yaikulu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Yoabu anatumiza ku Tekowa, natenga kumeneko mkazi wanzeru, nanena naye, Ukokomezeke monga mfedwa, nubvale zobvala za pamaliro, osadzola mafuta, koma ukhale ngati munthu wamkazi wakulira akufa nthawi yaikuru.