2 Samuel 14:22 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Yowabu adaŵerama pansi, adalambira mfumu, naithokoza. Tsono adati, “Tsopano ndadziŵa kuti inu mbuyanga mfumu mwandikomera mtima, chifukwa mwavomera pempho langali.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Yowabu anagwa nkhope yake pansi, namlambira, nadalitsa mfumuyo; nati Yowabu, Lero mnyamata wanu ndadziwa kuti munandikomera mtima, mbuye wanga mfumu, popeza mfumu yachita chopempha mnyamata wake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Yoabu anagwa nkhope yace pansi, namlambira, nadalitsa mfumuyo; nati Yoabu, Lero mnyamata wanu ndadziwa kuti munandikomera mtima, mbuye wanga mfumu, popeza mfumu yacita copempha mnyamata wace.