2 Samuel 14:30 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamenepo Abisalomu adauza atumiki ake kuti, “Munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga, ndipo ali ndi barele m'menemo. Pitani kautentheni.” Pompo atumiki a Abisalomu adapita kukautentha mundawo.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Chifukwa chake iye anati kwa anyamata ake, Onani munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga, ndipo iye ali ndi barele pamenepo, mukani mukamtenthere. Ndipo anyamata a Abisalomu anatentha za m'mundawo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Cifukwa cace iye anati kwa anyamata ace, Onani munda wa Yoabu uli pafupi ndi wanga, ndipo iye ali ndi barele pamenepo, mukani mukamtenthere. Ndipo anyamata a Abisalomu anatentha za m'mundawo.