2 Samuel 2:5 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
adatuma amithenga kwa anthuwo kukaŵauza kuti, “Chauta akudalitseni, poti mudaonetsa kukhulupirika kwanu pomuika Saulo mbuyanu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo Davide anatumiza mithenga kwa anthu a ku Yabesi-Giliyadi, nanena nao, Mudalitsike ndi Yehova inu, popeza munachitira chokoma ichi mbuye wanu Saulo, ndi kumuika.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
iye anatuma amithenga kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti akayankhule nawo kuti, “Yehova akudalitseni poonetsa kukoma mtima kwanu kwa Sauli mbuye wanu pomuyika mʼmanda.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo Davide anatumiza mithenga kwa anthu a ku Jabezi Gileadi, nanena nao, Mudalitsike ndi Yehova inu, popeza munacitira cokoma ici mbuye wanu Sauli, ndi kumuika.