2 Samuel 20:1 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Zidangochitika kuti kumeneko kunali munthu wina wachabechabe dzina lake Sheba, mwana wa Bikiri wa fuko la Benjamini. Iyeyo tsiku lina adaliza lipenga, nati, “Ife tilibe chathu mu ufumu wa Davide, tilibe choloŵa mwa mwana wa Yese! Inu Aisraele, aliyense apite kunyumba kwake!”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo kudangotero kuti pamenepo panali munthu woipa, dzina lake ndiye Sheba mwana wa Bikiri Mbenjamini; naliza iye lipenga, nati, Ife tilibe gawo mwa Davide, tilibenso cholowa mwa mwana wa Yese; munthu yense apite ku mahema ake, Israele inu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndipo munthu wina wokonda kuyambitsa chisokonezo, dzina lake Seba, mwana wa Bikiri wa fuko la Benjamini, anali komweko. Iye analiza lipenga ndipo anafuwula kuti, “Ife tilibe chathu mu mfumu wa Davide, tilibe gawo mwa mwana wa Yese! Inu Aisraeli aliyense apite ku nyumba kwake!”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo kudangotero kuti pamenepo panali munthu woipa, dzina lace ndiye Seba mwana wa Bikri Mbenjamini; naliza iye lipenga, nati, Ife tiribe gawo mwa Davide, tiribenso colowa mwa mwana wa Jese; munthu yense apite ku mahema ace, Israyeli inu.