2 Samuel 21:17 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma Abisai, mwana wa Zeruya, adabwera kudzathandiza Davide, nalimbana ndi Mfilistiyo mpaka kumupha. Tsono anthu a Davide adamlonjeza molumbira Davideyo kuti, “Tsopano inu simudzapita nafenso ku nkhondo, kuwopa kuti mungaphedwe. Inu ndinu amene Aisraele onse amagonerapo.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma Abisai mwana wa Zeruya anamthandiza namkantha Mfilistiyo, namupha. Pomwepo anthu a Davide anamlumbirira iye nati, Inu simudzatuluka nafenso kunkhondo, kuti mungazime nyali ya Israele.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma Abisai mwana wa Zeruya anabwera kudzapulumutsa Davide. Iye anamukantha Mfilisitiyo ndi kumupha. Pamenepo asilikali a Davide analumbira kwa iye kuti, “Inu simudzapita nafenso ku nkhondo, kuti nyale ya Israeli isadzazimitsidwe.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma Abisai mwana wa Zeruya anamthandiza namkantha Mfliistiyo, namupha. Pomwepo anthu a Davide anamlumbirira iye nati, Inu simudzaturuka nafenso kunkhondo, kuti mungazime nyali ya Israyeli.