2 Samuel 3:24 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Atamva zimenezo Yowabu adapita kwa mfumu nakafunsa kuti, “Inu amfumu, kodi akuti mwachita zotani? Abinere wobwera bwinobwino kuno, nanga bwanjinso inu mwamlola kuti apite? Moti wapitadi?
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pomwepo Yowabu anadza kwa mfumu, nati, Mwachitanji? Taonani, Abinere anadza kwa inu, chifukwa ninji tsono munalawirana naye kuti achokedi.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pomwepo Yoabu anadza kwa mfumu, nati, Mwacitanji? Taonani, Abineri anadza kwa inu, cifukwa ninji tsono munalawirana naye kuti acokedi.