Acts 19:26 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mukuwona ndi kumva zimene akuchita mkulu uyu amati Pauloyu. Iye akunena kuti ati milungu yopangidwa ndi anthu si milungu konse. Ndipo wakopa anthu ambiri nkuŵapatutsa, osati ku Efeso kokha kuno ai, komanso pafupi dziko lonse la Asiya.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo muona ndi kumva, kuti si pa Efeso pokha, koma monga pa Asiya ponse, Paulo uyu akopa ndi kutembenutsa anthu ambiri, ndi kuti, Si milungu iyi imene ipangidwa ndi manja:
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndipo inu mukuona ndi kumva kuti munthu uyu Paulo wakopa ndi kusokoneza anthu ambiri a ku Efeso ndiponso pafupifupi dziko lonse la Asiya. Iye akunena kuti milungu yopangidwa ndi anthu si milungu ayi.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo muona ndi kumva, kuti si pa Efeso pokha, koma monga pa Asiya ponse, Paulo uyu akopa ndi kutembenutsa anthu ambiri, ndi kuti, Si milungu iyi imene ipangidwa ndi manja: