Acts 20:16 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Paulo anali atatsimikiza zolambalala Efeso, kuwopa kutaya nthaŵi ku dziko la Asiya. Ankafulumira kuti ngati nkotheka akakhale ali ku Yerusalemu pa tsiku la Pentekoste.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pakuti Paulo adatsimikiza mtima apitirire pa Efeso, angataye nthawi m'Asiya; pakuti anafulumira, ngati kutheka, akhale ku Yerusalemu tsiku la Pentekoste.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Paulo anali atatsimikiza kuti alambalale Efeso kuopa kutaya nthawi ku Asiya, pakuti ankafulumira kuti akafike ku Yerusalemu kuti ngati nʼkotheka kuti tsiku la Pentekosite akakhale ali ku Yerusalemu.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pakuti Paulo adatsimikiza mtima apitirire pa Efeso, angataye nthawi m'Asiya; pakuti anafulumira, ngati kutheka, akhale ku Yerusalemu tsiku la Pentekoste.