Acts 21:11 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Iyeyo adadza kwa ife, ali ndi lamba wa Paulo. Tsono adadzimanga mapazi ndi manja nati, “Mzimu Woyera akuti, ‘Mwiniwake lamba uyu Ayuda adzammanga chomwechi ku Yerusalemu, ndi kumpereka m'manja mwa akunja.’ ”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo anadza kwa ife natenga lamba la Paulo, nadzimanga yekha manja ndi mapazi, nati, Atero Mzimu Woyera, Munthu mwini lamba ili, adzammanga kotero Ayuda a m'Yerusalemu, nadzampereka m'manja a amitundu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Atafika kwa ife, anatenga lamba wa Paulo, nadzimanga naye manja ake ndi mapazi ake ndipo anati, “Mzimu Woyera akuti, ‘Mwini lambayu, Ayuda adzamumanga chomwechi ku Yerusalemu, ndipo adzamupereka mʼmanja mwa anthu a mitundu ina.’ ”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo anadza kwa ife natenga lamba la Paulo, nadzimanga yekha manja ndi mapazi, nati, Atero Mzimu Woyera, Munthu mwini lamba ili, adzammanga kotero Ayuda a m'Yerusalemu, nadzampereka m'manja a amitundu.