Acts 21:13 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma iye adati, “Bwanji mukulira ndi kufuna kunditayitsa mtima? Inetu ndili wokonzeka kumangidwa, ngakhalenso kukafera ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo Paulo anayankha, Muchitanji, polira ndi kundiswera mtima? Pakuti ndakonzeka ine si kumangidwa kokha, komatunso kufera ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma Paulo anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukulira ndi kunditayitsa mtima? Ndine wokonzeka osati kumangidwa kokha ayi, komanso kufa ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo Paulo anayankha, Mucitanji, polira ndi kundiswera mtima? pakuti ndakonzeka Ine si kumangidwa kokha, komatunso kufera ku Yerusalemu cifukwa ca dzina la Ambuye Yesu.