Acts 23:15 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono inu, pamodzi ndi Bwalo Lalikulu lamilandu, mutumize mau kwa mkulu wa asilikali kuti abwere naye Paulo kwa inu, ngati kuti mukufuna kufunsitsa bwino za mlandu wake. Ife tili okonzeka kudzamuphha asanafike kuno.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Potero tsopano inu ndi bwalo la akulu muzindikiritse kapitao wamkulu kuti atsike naye kwa inu, monga ngati mufuna kudziwitsitsa bwino za iye; koma tadzikonzeratu timuphe asanayandikire iye.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Tsopano inu pamodzi ndi akuluakulu a Bwalo Lalikulu mupemphe mkulu wa asilikali kuti akubweretsereni Paulo ngati kuti mukufuna kudziwa bwino za mlandu wake. Ife takonzeka kudzamupha asanafike kumeneko.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Potero tsopano inu ndi bwalo la akuru muzindikiritse kapitao wamkuru kuti atsikenaye kwa inu, monga ngati mufuna kudziwitsitsa bwino za iye; koma tadzikonzeratu timuphe asanayandikire iye.