Acts 28:23 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamenepo iwo adapangana naye tsiku, ndipo ambiri adaabwera kunyumba kumene iye ankakhala. Kuyambira m'maŵa mpaka madzulo Paulo adakhala akulankhula nawo, naŵafotokozera za ufumu wa Mulungu. Pakuŵatchulira mau a m'Malamulo a Mose ndiponso m'mabuku a aneneri, ankayesa kuŵakopa kuti akhulupirire Yesu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo pamene adampangira tsiku, anadza kunyumba yake anthu ambiri; amenewo anawafotokozera, ndi kuchitira umboni Ufumu wa Mulungu, ndi kuwakopa za Yesu, zochokera m'chilamulo cha Mose ndi mwa aneneri, kuyambira mamawa kufikira madzulo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Iwo anakonza tsiku lina loti akumane ndi Paulo, ndipo anabwera anthu ambiri ku nyumba kumene amakhala. Kuyambira mmawa mpaka madzulo, Paulo anawafotokozera ndi kuwawuza za ufumu wa Mulungu ndipo anayesa kuwakopa kuti akhulupirire Yesu kuchokera mʼMalamulo a Mose ndiponso mʼmabuku a Aneneri.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo pamene adampangira tsiku, anadza ku nyumba yace anthu ambiri; amenewo anawafotokozera, ndikucitira umboni Ufumu wa Mulungu, ndi kuwakopa za Yesu, zocokera m'cilamulo ca Mose ndi mwa aneneri, kuyambira mamawa kufikira madzulo.