Acts 28:4 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamene anthuwo adaona njokayo ili lende ku dzanja lake, adayamba kuuzana kuti, “Ndithudi munthu ameneyu nchigaŵenga. Ngakhale wapulumuka pa nyanja, koma Mulungu wachilungamo sadamlole kuti akhale ndi moyo.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma pamene akunjawo anaona chilombocho chili lende pa dzanja lake, ananena wina ndi mnzake, Zoona munthuyu ndiye wambanda. Angakhale anapulumuka m'nyanja, chilungamo sichimlola akhale ndi moyo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Anthu a pa chilumbacho ataona njokayo ili lende pa dzanja lake, iwo anawuzana kuti, “Munthu uyu akuyenera kukhala munthu wopha anthu; pakuti ngakhale wapulumuka pa nyanja, chilungamo sichinamulore kuti akhale ndi moyo.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma pamene akunjawo anaona ciromboco ciri lende pa dzanja lace, ananena wina ndi mnzace, Zoona munthuyu ndiye wambanda, angakhale anapulumuka m'nyanja, cilungamo sicimlola akhale ndi moyo.