Acts 9:27 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamenepo munthu wina, dzina lake Barnabasi, adamtenga napita naye kwa atumwi. Iye adaŵafotokozera za m'mene Saulo adaaonera Ambuye panjira paja, ndipo kuti Ambuye adaalankhula naye. Adaŵasimbiranso za m'mene Saulo ku Damasiko ankalankhulira molimba mtima m'dzina la Yesu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma Barnabasi anamtenga, napita naye kwa atumwi, nawafotokozera umo adaonera Ambuye m'njira, ndi kuti analankhula naye, ndi kuti m'Damasiko adanena molimbika mtima m'dzina la Yesu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma Barnaba anamutenga napita naye kwa atumwi. Iye anawafotokozera iwo za mmene Saulo anaonera Ambuye pa njira paja, ndi kuti Ambuye anamuyankhula, ndi momwe analalikira ku Damasiko mʼdzina la Yesu mosaopa.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma Bamaba anamtenga, napita naye kwa atumwi, nawafotokozera umo adaonera Ambuye m'njira, ndi kuti analankhula naye, ndi kuti m'Damasiko adanena molimbika mtima m'dzina la Yesu.