Amos 1:11 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Zimene akunena Chauta ndi izi: “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, sindileka kuŵalanga. Iwo adathamangitsa abale ao lupanga lili kumanja, popanda nchifundo chomwe. Ndiponso anali ndi ukali wosatonthozeka, ndi mkwiyo wosapozeka.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Edomu, kapena zinani, sindidzabweza kulanga kwake; popeza analondola mphwake ndi lupanga, nafetsa chifundo chake chonse, ndi mkwiyo wake unang'amba ching'ambire nasunga mkwiyo wake chisungire;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga, popanda nʼchifundo chomwe. Popeza mkwiyo wake unakulabe ndipo ukali wake sunatonthozeke,
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Edomu, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza analondola mphwace ndi lupanga, nafetsa cifundo cace conse, ndi mkwiyo wace unang'amba cing'ambire, nasunga mkwiyo wace cisungire;