Amos 1:6 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Zimene akunena Chauta ndi izi: “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, sindileka kuŵalanga. Iwo adatenga mtundu wathunthu wa anthu kunka nawo ku ukapolo, ndipo adaupereka ku Edomu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Gaza, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwake; popeza anatenga ndende anthu onse kuwapereka kwa Edomu;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu ndi kuwugulitsa ku Edomu,
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Gaza, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anatenga ndende anthu onse kuwapereka kwa Edomu;